01/06/2026
Bambo Bernado Khinda Chilichawo, a zaka 48 afa m'boma la Dowa atakomoka pa nthawi yogonana ndi chibwenzi chawo cha zaka 21, ndipo akuganiziridwa kuti anamwa chakumwa choonjezera mphamvu pogonana.
Mneneri wa Polisi ya Dowa, a Sub Inspector Alice Sitima atsimikiza za infayi, ndipo ati awiriwa anakalowa m'chipinda china pa malo ena ogona m'bomali, pomwe bamboyo anatuluka kaye kukagula mabotolo awiri a chakumwacho asanayambe kugonana.
A Sitima ati malemuyo atamwa botolo loyamba, zinthu zinayenda bwino koma atamwa botolo lachiwiri, bamboyo anakomoka mwadzidzidzi ndipo anatengeredwa ku chipatala komwe anamwalira ali mkati molandira chithandizo cha chipatala.
Zotsatira za kuchipatala zasonyeza kuti bamboyo anamwalira chifukwa cha matenda a mtima komanso kuthamanga kwa magazi komwe kukuganizilidwa kuti kunadza kaamba komwa mabotolo awiri owonjezera mphamvu.