14/11/2021
NAMADINGO WACHITA NGOZI
Oyimba odziwika bwino muno m'Malawi, Patience Namadingo adachita ngozi dzulo pa 13 November ku Chigumula, Blantyre.
Malingana ndi Kafukufuku wathu panthawiyi oyimbayu adali kuyendela galimoto ya ntundu wa (Mercedes Benz) ndipo atafika malo ena ku Chigumulako iye adalephera kuongolera bwino mpaka galeta lakeli lidalowa kuphompho.
Atafunsidwapo za Nkhaniyi, Dr Namadingo adanenena mophiphiritsa kuti " Galimoto yachita ngozi Ndiyangadi, Koma ine sindidali Mkatimo"
Ndipo nkhani yosangalatsa ndiyokuti Dr Namadingo sadavulare pa Ngoziyi.
-Naomi Kamiza